Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 8:40-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo pakubwera Yesu, khamu la anthu linamlandira iye; pakuti onse analikumlindira iye.

41. Ndipo onani, panadza munthu dzina lace Yairo, ndipo iye ndiye mkuru wa sunagoge; ndipo anagwa pamapazi ace a Yesu, nampempha iye adze kunyumba kwace;

42. cifukwa anali naye mwana wamkazi mmodzi yekha, wa zaka zace ngati khumi ndi ziwiri, ndipo analinkumwalira iye, Koma pakupita iye anthu a mipingo anakanikizana naye,

43. Ndipo mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, amene adasudzula asing'anga za moyo wace zonse, ndipo sanathe kuciritsidwa ndi mmodzi yense,

Werengani mutu wathunthu Luka 8