Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iye, Kwanenedwa,Usamuyese Ambuye Mulungu wako,

13. Ndipo mdierekezi, m'mene adamariza mayesero onse, analekana naye kufikira nthawi yina.

14. Ndipo Yesu anabwera ndi mphamvu ya Mzimu ku Galileya; ndipo mbiri yace ya iye inabuka ku dziko lonse loyandikira.

15. Ndipo iye anaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalemekezedwa ndi anthu onse.

16. Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo tsiku la Sabata analowa m'sunagoge, monga anazolowera, naimiriramo kuwerenga m'kalata.

17. Ndipo anapereka kwa iye buku la Yesaya mneneri. Ndipo m'mene iye adafunyulula bukulo, anapeza pomwe panalembedwa,

18. Mzimu wa Ambuye uli paine,Cifukwa cace iye anandidzozaIne ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino:Anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe,Ndi akhungu kuti apenyenso,Kuturutsa ndi ufuru ophwanyika,

Werengani mutu wathunthu Luka 4