Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 3:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo iye anadza ku dziko lonse la m'mbali mwa Yordano, nalalikira ubatizo wa kulapa mtima kuloza ku cikhululukiro ca macimo;

4. monga mwalembedwa m'kalata wa mau a Yesaya mneneri, kuti,Mau a wopfuula m'cipululu,Konzani khwalala la Ambuye,Lungamitsani njira zace.

5. Cigwa ciri conse cidzadzazidwa,Ndipo phiri liri lonse ndi mtunda uti wonse zidzacepsedwa;Ndipo zokhota zidzakhala zolungama,Ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala;

6. Ndipo anthu onse adzaona cipulumutso ca Mulungu.

7. Cifukwa cace iye ananena kwa makamuwo a anthu amene anaturukira kukabatizidwa ndi iye, Obadwa a njoka inu, anakulangizani inu ndani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8. Cifukwa cace balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.

9. Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cotero mtengo uli wonse wosabala cipatso cabwino udulidwa, nuponyedwa pamoto.

10. Ndipo anthu a makamu anamfunsa iye, nanena, Ndipo tsono tizicita ciani?

11. Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya acite comweco.

12. Ndipo amisonkho omwe anadza kudzabatizidwa, nati kwa iye, Mphunzitsi, ife tizicita ciani?

Werengani mutu wathunthu Luka 3