Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:36-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.

38. Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?

39. Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.

40. Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.

Werengani mutu wathunthu Luka 24