Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:34-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.

35. Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.

36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.

38. Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?

39. Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.

40. Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.

41. Koma pokhala iwo cikhalire osakhulupirira cifukwa ca cimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, 3 Muli nako kanthu kakudya kuno?

42. Ndipo anampatsa iye cidutsu ca nsomba yokazinga.

Werengani mutu wathunthu Luka 24