8. Ndipo Herode, pamene anaona Yesu, anakondwa ndithu; pakuti anayamba kale kufuna kumpenya iye, cifukwa anamva za iye; nayembekeza kuona cizindikilo cina cocitidwa ndi iye.
9. Ndipo anamfunsa iye mau ambiri; koma iye sanamyankha kanthu.
10. Ndipo ansembe akuru ndi alembi anaimirira, namnenera iye kolimba.
11. Ndipo Herode ndi asilikari ace anampeputsa iye, namnyoza, nambveka iye copfunda conyezimira, nambwezera kwa Pilato.