Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:49-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Ndipo 3 omdziwa iye onse, ndi akazi amene adamtsata kucokera ku Galileya, anaima kutari, naona zinthu izi.

50. Ndipo taonani, munthu dzina lace Yosefe, ndiye mkuru wa mirandu, munthu wabwino ndi wolungama

51. (amene sanabvomereza kuweruza kwao ndi nchito yao) wa ku Arimateya, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,

52. yemweyo anapita kwa Pilato napempha mtembo wace wa Yesu.

53. Ndipo 4 anautsitsa, naukulunga m'nsaru yabafuta, nauika m'manda osemedwa m'mwala, m'menemo sanaika munthu ndi kale lonse.

Werengani mutu wathunthu Luka 23