Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:46-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Ndipo pamene Yesu anapfuula ndi mau akuru, anati, 1 Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wace.

47. Ndipo 2 pamene kenturiyo anaona cinacitikaco, analemekeza Mulungu, nanena, Zoonadi munthu uyu anali wolungama.

48. Ndipo makamu onse osonkhana kudzapenya ici, pamene anaona zinacitikazo, anapita kwao ndi kudziguguda pacifuwa.

49. Ndipo 3 omdziwa iye onse, ndi akazi amene adamtsata kucokera ku Galileya, anaima kutari, naona zinthu izi.

50. Ndipo taonani, munthu dzina lace Yosefe, ndiye mkuru wa mirandu, munthu wabwino ndi wolungama

51. (amene sanabvomereza kuweruza kwao ndi nchito yao) wa ku Arimateya, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,

52. yemweyo anapita kwa Pilato napempha mtembo wace wa Yesu.

53. Ndipo 4 anautsitsa, naukulunga m'nsaru yabafuta, nauika m'manda osemedwa m'mwala, m'menemo sanaika munthu ndi kale lonse.

54. Ndipo panali tsiku lokonzera, ndi Sabata linayandikira.

Werengani mutu wathunthu Luka 23