Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Cifukwa taonani masiku alinkudza, pamene adzati, Odala ali ouma ndi mimba yosabala, ndi mawere osayamwitsa.

30. Pomwepo adzayamba kunena kwa mapiri, Igwani pa ife; ndi kwa zitunda, Bisani ife.

31. Pakuti ngati azicitira izi mtengo wauwisi, nanga kudzatani ndi wouma?

32. Ndipo analinso awiri ena, ndiwo ocita zoipa; anatengedwa pamodzi ndi iye kuti aphedwe.

33. Ndipo pamene anafika ku malo dzina lace Bade, anampacika iye pamtanda pomwepo, ndi ocita zoipa omwe, mmodzi ku dzanja lamanja ndi wina kulamanzere.

Werengani mutu wathunthu Luka 23