Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. ]

18. Koma iwo onse pamodzi anapfuula, nati, Cotsani munthu uyu, mutimasulire Baraba;

19. ndiye munthu anaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko m'mudzi ndi ca kupha munthu.

20. Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;

21. koma iwo anapfuula, nanena, Mpacikeni, mpacikeni pamtanda.

22. Ndipo anati kwa iwo nthawi yacitatu, Nanga munthuyu anacita coipa ciani? Sindinapeza cifukwa ca kufera iye; cotero ndidzamkwapula iye ndi kummasula.

23. Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti iye apacikidwe, Ndipo mau ao analakika.

Werengani mutu wathunthu Luka 23