11. Ndipo Herode ndi asilikari ace anampeputsa iye, namnyoza, nambveka iye copfunda conyezimira, nambwezera kwa Pilato.
12. Ndipo Herode ndi Pilato anaci-I tana cibwenzi tsiku lomwelo; pakuti kale anadana.
13. Ndipo Pilato anaitana ansembe akuru, ndi akuru, ndi anthu, asonkhane,
14. nati kwa iwo, Munadza kwa ine ndi munthu uyu ngati munthu wakupandutsa anthu: ndipo taonani, Ine ndinamfunsa za mlanduwu pamaso panu, ndipo sindinapeza pa munthuyu cifukwa ca zinthu zimene mumnenera;
15. inde, nga khale Herode yemwe; pakuti iye anambwezera iye kwa ife; ndipo taonani, sanacita iye kanthu kakuyenera kufa.
16. Cifukwacace ndidzamkwapula ndi kununasula iye. [
17. ]
18. Koma iwo onse pamodzi anapfuula, nati, Cotsani munthu uyu, mutimasulire Baraba;
19. ndiye munthu anaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko m'mudzi ndi ca kupha munthu.
20. Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;
21. koma iwo anapfuula, nanena, Mpacikeni, mpacikeni pamtanda.
22. Ndipo anati kwa iwo nthawi yacitatu, Nanga munthuyu anacita coipa ciani? Sindinapeza cifukwa ca kufera iye; cotero ndidzamkwapula iye ndi kummasula.
23. Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti iye apacikidwe, Ndipo mau ao analakika.