Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo ansembe akuru ndi alembi anaimirira, namnenera iye kolimba.

11. Ndipo Herode ndi asilikari ace anampeputsa iye, namnyoza, nambveka iye copfunda conyezimira, nambwezera kwa Pilato.

12. Ndipo Herode ndi Pilato anaci-I tana cibwenzi tsiku lomwelo; pakuti kale anadana.

13. Ndipo Pilato anaitana ansembe akuru, ndi akuru, ndi anthu, asonkhane,

14. nati kwa iwo, Munadza kwa ine ndi munthu uyu ngati munthu wakupandutsa anthu: ndipo taonani, Ine ndinamfunsa za mlanduwu pamaso panu, ndipo sindinapeza pa munthuyu cifukwa ca zinthu zimene mumnenera;

15. inde, nga khale Herode yemwe; pakuti iye anambwezera iye kwa ife; ndipo taonani, sanacita iye kanthu kakuyenera kufa.

16. Cifukwacace ndidzamkwapula ndi kununasula iye. [

Werengani mutu wathunthu Luka 23