Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:51-55 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Koma Yesu anayankha nati, Lolani kufikira kumene. Ndipo anakhudza khutu lace, namciritsa.

52. Ndipo 5 Yesu anati kwa ansembe akulu ndi akapitao a Kacisi, ndi akuru, amene anadza kumgwira iye, Munaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kodi monga ngati kugwira wacifwamba?

53. Masiku onse, pamene ndinali ndi inu m'Kacisi, simunatansa manja anu kundigwira: koma 6 nyengo yino ndi yanu, ndipo ulamuliro wa mdima ndi wanu.

54. Ndipo 7 pamenepo anamgwira iye, napita naye, nalowa m'nyumba ya mkulu wa ansembe. Koma Petro anatsata kutari.

55. Ndipo 8 pamene adasonkha mota m'kati mwa bwalo, nakhala pansi pamodzi, Petro anakhala pakati pao.

Werengani mutu wathunthu Luka 22