Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:49-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Ndipo m'mene iwo akumzinga iye anaona cimene citi cicitike, anati, Ambuye, tidzakantha ndi lupanga kodi?

50. Ndipo wina wa iwo 4 anakantha kapolo wa mkuru wa ansembe, namdula khutu lace lamanja.

51. Koma Yesu anayankha nati, Lolani kufikira kumene. Ndipo anakhudza khutu lace, namciritsa.

52. Ndipo 5 Yesu anati kwa ansembe akulu ndi akapitao a Kacisi, ndi akuru, amene anadza kumgwira iye, Munaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kodi monga ngati kugwira wacifwamba?

53. Masiku onse, pamene ndinali ndi inu m'Kacisi, simunatansa manja anu kundigwira: koma 6 nyengo yino ndi yanu, ndipo ulamuliro wa mdima ndi wanu.

Werengani mutu wathunthu Luka 22