Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:47-66 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. Pamene iye anali cilankhulire, taonani, khamu la anthu, ndipo iye wochedwa Yudase, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anawatsogolera; nayandikira Yesu kumpsompsona iye.

48. Koma Yesu anati kwa iye, Yudase, ulikupereka Mwana wa munthu ndi cimpsompsono kodi?

49. Ndipo m'mene iwo akumzinga iye anaona cimene citi cicitike, anati, Ambuye, tidzakantha ndi lupanga kodi?

50. Ndipo wina wa iwo 4 anakantha kapolo wa mkuru wa ansembe, namdula khutu lace lamanja.

51. Koma Yesu anayankha nati, Lolani kufikira kumene. Ndipo anakhudza khutu lace, namciritsa.

52. Ndipo 5 Yesu anati kwa ansembe akulu ndi akapitao a Kacisi, ndi akuru, amene anadza kumgwira iye, Munaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kodi monga ngati kugwira wacifwamba?

53. Masiku onse, pamene ndinali ndi inu m'Kacisi, simunatansa manja anu kundigwira: koma 6 nyengo yino ndi yanu, ndipo ulamuliro wa mdima ndi wanu.

54. Ndipo 7 pamenepo anamgwira iye, napita naye, nalowa m'nyumba ya mkulu wa ansembe. Koma Petro anatsata kutari.

55. Ndipo 8 pamene adasonkha mota m'kati mwa bwalo, nakhala pansi pamodzi, Petro anakhala pakati pao.

56. Ndipo mdzakazi anamuona iye alikukhala m'kuwala kwace kwa moto, nampenyetsa iye, nati, Munthu uyunso anali naye.

57. Koma anakana, nati, Mkaziwe, sindimdziwa iye.

58. Ndipo 9 popita kamphindi, anamuona wina, nati, Iwenso uli mmodzi wa awo. Koma Petro anati, Munthu iwe, sindine.

59. Ndipo 10 patapita ngati ora limodzi, wina ananenetsa, kuti, Zoonadi, munthu uyunso anali naye, pakuti ndiye Mgalileya.

60. Koma Petro anati, Munthu iwe, sindidziwa cimene ucinena, Ndipo pomwepo, iye ali cilankhulire, tambala analira.

61. Ndipo Ambuye anapotoloka, nayang'ana Petro. Ndipo 11 Petra anakumbukila mau a Ambuye, kuti anati kwa iye, 12 Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.

62. Ndipo anaturuka, nalira misozi ndi kuwawa mtima.

63. Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza iye, nampanda.

64. Ndipo anamkulunga iye m'maso, namfunsa, nati, Talota; anakupanda Iwe ndani?

65. Ndipo zambiri zina anamnenera iye, namcitira mwano.

66. Ndipo 13 pamene kunaca, bungwe la akuru a anthu linasonkhana, ndiwo ansembe akuru ndi alembi; ndipo anapita naye ku bwalo lao, nanena, 14 Ngati uli Kristu, utiuze.

Werengani mutu wathunthu Luka 22