Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:42-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. nati, Atate, mukafuna Inu, cotsani cikho ici pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kucitike.

43. Ndipo anamuonekera iye 1 mngelo wa Kumwamba namlimbitsa iye.

44. Ndipo 2 pokhala iye m'cipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lace linakhala ngati madontho akuru a mwazi alinkugwa pansi.

45. Ndipo pamene ananyamuka pakupemphera anadza kwa ophunzira, nawapeza ali m'tulo ndi cisoni,

46. ndipo anati kwa iwo, Mugoneranji? Ukani, 3 pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.

47. Pamene iye anali cilankhulire, taonani, khamu la anthu, ndipo iye wochedwa Yudase, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anawatsogolera; nayandikira Yesu kumpsompsona iye.

48. Koma Yesu anati kwa iye, Yudase, ulikupereka Mwana wa munthu ndi cimpsompsono kodi?

Werengani mutu wathunthu Luka 22