Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:29-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. ndipo Ine ndikuikirani ufumu, monganso Atate wanga anandiikira Ine, kuti mukadye ndi kumwa kugome kwanga mu Ufumu wanga;

30. ndipo mudzakhala pa mipando yacifumu ndi kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

31. Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu;

32. koma ndinakupempherera kuti cikhulupiriro cako cingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

33. Ndipo anati kwa iye, Ambuye, ndiripo ndikapite ndi Inu kundende ndikuimfa.

34. Ndipo iye anati, Ndikuuza iwe, Petro, sadzalira tambala lero lino kufikira udzakana katatu kuti sundidziwa Ine.

35. Ndipo anati kwa iwo, Pamene ndinakutumizani opanda thumba la ndalama, ndi thumba la kamba, ndi nsapato, munasowa kanthu kodi? Anati iwo, Iai.

36. Ndipo anati kwaiwo, Koma tsopano, iye amene ali ndi thumba la ndalama, alitenge, ndi thumba la kamba lomwe; ndipo amene alibe, agulitse copfunda cace, nagule lupanga,

37. Pakuti ndinena ndi inu, cimene cidalembedwa ciyenera kukwanitsidwa mwa Ine, Ndipo anawerengedwa ndi anthu opanda lamulo; pakuti izi za kwa Ine ziri naco cimariziro.

38. Ndipo iwo anati, Ambuye, taonani, malupanga awir siwa. Ndipo anati kwa iwo, Cakwa nira.

39. Ndipo iye anaturuka, napita monga adafucita, ku phiri la Azitona ndi ophunzira anamtsata iye.

40. Ndipo pofika pomwepo, anati kwa iwo, Pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.

41. Ndipo anapatukana nao kutalika kwace ngan kuponya mwala, nagwada pansi napemphera,

42. nati, Atate, mukafuna Inu, cotsani cikho ici pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kucitike.

43. Ndipo anamuonekera iye 1 mngelo wa Kumwamba namlimbitsa iye.

44. Ndipo 2 pokhala iye m'cipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lace linakhala ngati madontho akuru a mwazi alinkugwa pansi.

45. Ndipo pamene ananyamuka pakupemphera anadza kwa ophunzira, nawapeza ali m'tulo ndi cisoni,

Werengani mutu wathunthu Luka 22