Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:28-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Koma inu ndinuamene munakhala ndi Ine cikhalire m'mayesero anga;

29. ndipo Ine ndikuikirani ufumu, monganso Atate wanga anandiikira Ine, kuti mukadye ndi kumwa kugome kwanga mu Ufumu wanga;

30. ndipo mudzakhala pa mipando yacifumu ndi kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

31. Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu;

32. koma ndinakupempherera kuti cikhulupiriro cako cingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

33. Ndipo anati kwa iye, Ambuye, ndiripo ndikapite ndi Inu kundende ndikuimfa.

34. Ndipo iye anati, Ndikuuza iwe, Petro, sadzalira tambala lero lino kufikira udzakana katatu kuti sundidziwa Ine.

Werengani mutu wathunthu Luka 22