Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo kunakhala kutsutsana mwa iwo, ndani wa iwo ayesedwe wamkuru.

25. Ndipo anati kwa iwo, Mafumu a anthu a mitundu awacitira ufumu; ndipo iwo amene awacitira ulamuliro anenedwa, Ocitira zabwino.

26. Koma sipadzatero ndi inu; komatu iye ali wamkuru mwa inu, akhale ngati wamng'ono; ndi iye ali woyamba, akhale ngati wotumikira.

27. Pakuti wamkuru ndani, iye wakuseama pacakudya kapena wakutumikirapo? si ndiye wakuseama pacakudya kodi? koma Ine ndiri pakati pa inu monga ngati wotumikira.

28. Koma inu ndinuamene munakhala ndi Ine cikhalire m'mayesero anga;

Werengani mutu wathunthu Luka 22