Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 22:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anapita iwo, napeza monga adatero nao; ndipo anakonza Paskha.

14. Ndipo itadza nthawi yace, iye anakhala pacakudya, ndi ophunzira pamodzi ndi iye.

15. Ndipo anati kwa iwo, Ndinalakalaka ndithu kudya Paskha uwu pamodzi ndinu, ndisanayambe kusautsidwa;

16. pakuti ndinena ndi inu, sindidzadya kufikira udzakwaniridwa mu Ufumu wa Mulungu.

17. Ndipo analandira cikho, ndipo pamene adayamika, anati, Landirani ici, mucigawane mwa inu nokha;

18. pakuti ndinena kwa inu, kuyambira tsopano Ine sindidzamwako cipatso ca mpesa, kufikira Ufumu wa Mulungu udzafika.

19. Ndipo m'mene adatenga mkate, nayamika, anaunyema, nawapatsa, nanena, ici ndi thupi langa lopatsidwa cifukwa ca inu; citani ici cikumbukilo canga.

20. Ndipo coteronso cikho, atatha mgonero, nanena, Cikho ici ndi pangano latsopano m'mwazi wanga wothiridwa cifukwa ca inu.

21. Koma onani, dzanja lace la iye amene adzandipereka ali pagome pano pamodzi ndi Ine.

Werengani mutu wathunthu Luka 22