Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 20:34-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ana a dziko lapansi akwatira nakwatiwa:

35. koma iwo akuyesedwa oyenera kufikira dzikolijalo, ndi kuuka kwa akufa, sakwatira kapena kukwatiwa.

36. Pakuti sangathe kufanso nthawi zonse; pakuti afanafana ndi angelo; ndipo ali ana a Mulungu, popeza akhala ana a kuuka kwa akufa.

37. Koma za kuti anthu akufa auka, anasonyeza ngakhale Mose, pa Citsamba cija, pamene iye amchulira Ambuye, Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.

38. Ndipo iye sakhala Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: pakuti anthu onse akhala ndi moyo kwa iye.

39. Ndipo alembi ena anayankha nati, Mphunzitsi, mwanena bwino.

40. Pakuti sanalimbanso mtima kumfunsa iye kanthu kena.

41. Koma iye anati kwa iwo, Amanena bwanji kuti Kristuyo ndiye mwana wa Davine?

42. Pakuti Davine yekha anena m'buku la Masalmo,Ambuye ananena kwa Ambuye wanga,Ukhale pa dzanja langa lamanja,

43. Kufikira Ine ndikaika adani akopansi pa mapazi ako.

44. Cotero Davine anamchula iye Ambuye, ndipo nanga ali mwana wace bwanji?

45. Ndipo pamene anthu onse anallinkumva iye, anati kwa ophunzira,

46. Cenjerani nao alembi, amene afuna kuyendayenda obvala miinjiro, nakonda kulankhulidwa m'misika, ndi mipando yaulemu m'sunagoge, ndi malo aulemu pamapwando;

47. amene aononga nyumba za akazi amasiye, ndipo monyenga acita mai pemphero atali; amenewo adzalandira kulanga koposa.

Werengani mutu wathunthu Luka 20