2. ndipo anati, nanena naye, Mutiuze mucita in ndi ulamuliro wotani? Kapena ndani iye amene anakupatsani ulamuliro umene?
3. Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Ndidzakufunsani mau Inenso; mundiuze:
4. Ubatizo wa Yohane unacokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu?
5. Ndipo anatsutsana mwa okha, nanena, Ngati tinena ucokera Kumwamba; adzati, Simunamkhulupirira cifukwa ninji?
6. ndiponso, tikanena, Ucokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane ali mneneri.
7. Ndipo anayankha kuti sadziwa kumene ucokera.
8. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndingakhale Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu izi.