Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 20:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo anati, nanena naye, Mutiuze mucita in ndi ulamuliro wotani? Kapena ndani iye amene anakupatsani ulamuliro umene?

3. Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Ndidzakufunsani mau Inenso; mundiuze:

4. Ubatizo wa Yohane unacokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu?

5. Ndipo anatsutsana mwa okha, nanena, Ngati tinena ucokera Kumwamba; adzati, Simunamkhulupirira cifukwa ninji?

6. ndiponso, tikanena, Ucokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane ali mneneri.

7. Ndipo anayankha kuti sadziwa kumene ucokera.

8. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndingakhale Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu izi.

Werengani mutu wathunthu Luka 20