Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 20:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo anatumizanso kapolo wina; ndipo iyenso anampanda, namcitira cipongwe, nambweza, wopanda kanthu.

12. Ndipo anatumizanso wina wacitatu; ndipo iyenso anamlasa, namtaya kunja.

13. Ndipo mwini mundawo anati, Ndidzacita ciani? Ndidzatuma mwana wanga amene ndikondana naye; kapena akamcitira iye ulemu.

14. Koma olimawo, pamene anamuona, anauzana wina ndi mnzace, nati, Uyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe, kuti colowa cace cikhale cathu.

15. Ndipo anamponya kunja kwa mundawo, namupha, Pamenepo mwini munda wamphesawo adzawacitira ciani?

16. iye adzafika nadzaononga olima munda aja, nadzapatsa munda kwa ena. Ndipo pamene iwo anamva, anati, Musatero iail

Werengani mutu wathunthu Luka 20