Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 20:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali lina la masiku awo m'mene iye analikuphunzitsa anthu m'Kacisi, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, adamdzera ansembe akulu ndi alembi pamodzi ndi akulu;

2. ndipo anati, nanena naye, Mutiuze mucita in ndi ulamuliro wotani? Kapena ndani iye amene anakupatsani ulamuliro umene?

3. Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Ndidzakufunsani mau Inenso; mundiuze:

4. Ubatizo wa Yohane unacokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu?

5. Ndipo anatsutsana mwa okha, nanena, Ngati tinena ucokera Kumwamba; adzati, Simunamkhulupirira cifukwa ninji?

Werengani mutu wathunthu Luka 20