Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:9-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo mngelo wa Ambuye anaimirira pa awo, ndi kuwala kwa Ambuye kunawaunikira kozungulira: ndipo anaopa ndi mantha akuru.

10. Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa cikondwero cacikuru, cimene cidzakhala kwa anthu onse;

11. pakuti wakubadwirani inu lero, m'mudzi wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Kristu Ambuye.

12. Ndipo ici ndi cizindikilo kwa inu: Mudzapeza mwana wakhanda wokuta ndi nsaru atagonamodyera.

13. Ndipo dzidzidzi panali pamodzi ndi mngeloyo ambirimbiri a gulu la Kumwamba, natamanda Mulungu, nanena,

14. Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba,Ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

15. Ndipo panali, pamene angelo anacokera kwa iwo kunka Kumwamba, abusa anati wina ndi mnzace, Tipitiretu ku Betelehemu, tikaone cinthu ici cidacitika, cimene Ambuye anatidziwitsira ife.

16. Ndipo iwo anadza ndi cangu, napeza Mariya, ndi Yosefe, ndi mwana wakhanda atagona modyera.

17. Ndipo iwo, m'mene anaona, anadziwitsa anthu za mau analankhulidwa kwa iwo a mwana uyu.

18. Ndipo anthu onse amene anamva anazizwa ndi zinthu abusa adalankhula nao.

19. Koma Mariya anasunga mau awa onse, nawalingalira mumtima mwace.

20. Ndipo abusawo anabwera, nalemekeza ndi kutamanda Mulungu pa zinthu zonse anazimva, naziona, monga kunalankhulidwa kwa iwo.

21. Ndipo pamene panakwanira masiku asanu ndi atatu akumdula iye, anamucha dzina lace Yesu, limene anachula mngeloyo asanalandiridwe iye m'mimba.

22. Ndipo pamene anakwanira masiku a kukonza kwao, monga mwa cilamulo ca Mose, iwo anakwera naye kunka ku Yerusalemu, kukamsonyeza iye kwa Ambuye,

23. (monga mwalembedwa m'cilamulo ca Ambuye, kuti mwamuna ali yense wotsegula pa mimba ya amace adzanenedwa wopatulika wa kwa Ambuye)

Werengani mutu wathunthu Luka 2