28. pomwepo iye anamlandira iye m'manja mwace, nalemekeza Mulungu, nati,
29. Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja,Lolani ine, kapolo wanu, ndicoke mumtendere;
30. Cifukwa maso anga adaona cipulumutso canu,
31. Cimene munakonza pamaso pa anthu onse,
32. Kuunika kukhale cibvumbulutso ca kwa anthu a mitundu,Ndi ulemerero wa anthu anu Israyeli.
33. Ndipo atate ndi amace anali kuzizwa ndi zinthu zolankhulidwa za iye.