Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:28-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. pomwepo iye anamlandira iye m'manja mwace, nalemekeza Mulungu, nati,

29. Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja,Lolani ine, kapolo wanu, ndicoke mumtendere;

30. Cifukwa maso anga adaona cipulumutso canu,

31. Cimene munakonza pamaso pa anthu onse,

32. Kuunika kukhale cibvumbulutso ca kwa anthu a mitundu,Ndi ulemerero wa anthu anu Israyeli.

33. Ndipo atate ndi amace anali kuzizwa ndi zinthu zolankhulidwa za iye.

Werengani mutu wathunthu Luka 2