Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo pamene anakwanira masiku a kukonza kwao, monga mwa cilamulo ca Mose, iwo anakwera naye kunka ku Yerusalemu, kukamsonyeza iye kwa Ambuye,

23. (monga mwalembedwa m'cilamulo ca Ambuye, kuti mwamuna ali yense wotsegula pa mimba ya amace adzanenedwa wopatulika wa kwa Ambuye)

24. ndi kukapereka nsembe monga mwanenedwa m'citamulo ca Ambuye, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri.

25. Ndipo onani, m'Yerusalemu munali munthu, dzina lace Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israyeli; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.

26. Ndipo anamuululira Mzimu Woyera kuti sadzaona imfa, kufikira adzaona Kristu wace wa Ambuye.

Werengani mutu wathunthu Luka 2