Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:21-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo pamene panakwanira masiku asanu ndi atatu akumdula iye, anamucha dzina lace Yesu, limene anachula mngeloyo asanalandiridwe iye m'mimba.

22. Ndipo pamene anakwanira masiku a kukonza kwao, monga mwa cilamulo ca Mose, iwo anakwera naye kunka ku Yerusalemu, kukamsonyeza iye kwa Ambuye,

23. (monga mwalembedwa m'cilamulo ca Ambuye, kuti mwamuna ali yense wotsegula pa mimba ya amace adzanenedwa wopatulika wa kwa Ambuye)

24. ndi kukapereka nsembe monga mwanenedwa m'citamulo ca Ambuye, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri.

25. Ndipo onani, m'Yerusalemu munali munthu, dzina lace Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israyeli; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.

26. Ndipo anamuululira Mzimu Woyera kuti sadzaona imfa, kufikira adzaona Kristu wace wa Ambuye.

27. Ndipo iye analowa kuKacisi ndi Mzimu: ndipo pamene atate ndi amace analowa ndi kamwanako Yesu, kudzamcitira iye mwambo wa cilamulo,

28. pomwepo iye anamlandira iye m'manja mwace, nalemekeza Mulungu, nati,

29. Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja,Lolani ine, kapolo wanu, ndicoke mumtendere;

30. Cifukwa maso anga adaona cipulumutso canu,

31. Cimene munakonza pamaso pa anthu onse,

32. Kuunika kukhale cibvumbulutso ca kwa anthu a mitundu,Ndi ulemerero wa anthu anu Israyeli.

33. Ndipo atate ndi amace anali kuzizwa ndi zinthu zolankhulidwa za iye.

34. Ndipo Simeoni anawadalitsa, nati kwa Mariya amace, Taona, Uyu waikidwa akhale kugwa ndi kunyamuka kwa anthu ambiri mwa. Israyeli; ndipo akhale cizindikilo cakutsutsana naco;

35. eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m'mitima yambiri akaululidwe.

36. Ndipo panali Anna, mneneri wamkazi, mwana wa Fanueli, wa pfuko la Aseri; amene anali wokalamba ndithu, nakhala ndi mwamuna wace, kuyambira pa unamwali wace,

Werengani mutu wathunthu Luka 2