Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:43-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Pakuti masiku adzakudzera, ndipo adani ako adzakuzingira linga, nadzakuzungulira iwe kwete, nadzakutsekereza ponsepo;

44. ndipo adzakupasula iwe, ndi ana ako mwa iwe; ndipo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa mwala unzace; popeza sunazindikira nyengo, ya mayang'aniridwe ako.

45. Ndipo analowa m'Kacisi, nayamba kuturutsa iwo akugulitsa malonda, nanena nao,

46. Kwalembedwa, Ndipo nyumba yanga idzakhala nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa iyo phanga la acifwamba.

47. Ndipo analikuphunzitsa m'Kacisi tsiku ndi tsiku. Koma ansembe akulu, ndi alembi ndi akulu a anthu anafunafuna kumuononga iye;

48. ndipo sanapeza cimene akacita; pakuti anthu onse anamlendewera iye kuti amve.

Werengani mutu wathunthu Luka 19