Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:30-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. nati, Mukani ku mudzi uli pandunji panu; m'menemo, polowa, mudzapeza mwana wa buru womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iri yonse; mummasule iye nimumtenge.

31. Ndipomunthuakati kwa inu, Mummasuliranji? mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32. Ndipo anacoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

33. Ndipo pamene anamasula mwana wa buru, eni ace anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa buru?

34. Ndipo anati, Ambuye amfuna iye.

35. Ndipo anadzanave kwa Yesu; ndipo anayalika zobvala zao pa mwana wa buruyo, nakwezapo Yesu.

36. Ndipo pakupita iye, anayala zobvala zao m'njira.

37. Ndipo pakuyandikira iye tsono potsetsereka pace pa phiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau akuru, cifukwa ca nchito zonse zamphamvu anaziona;

38. nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m'dzina la Ambuye; mtendere m'Mwamba, ndi ulemerero m'Mwambamwamba.

39. Ndipo Afarisi ena a m'khamu la anthu anati kwa iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu.

Werengani mutu wathunthu Luka 19