Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:28-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo m'mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

29. Ndipo kunali, m'mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri lochedwa la Azitona, anatuma awiri a ophunzira,

30. nati, Mukani ku mudzi uli pandunji panu; m'menemo, polowa, mudzapeza mwana wa buru womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iri yonse; mummasule iye nimumtenge.

31. Ndipomunthuakati kwa inu, Mummasuliranji? mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32. Ndipo anacoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

33. Ndipo pamene anamasula mwana wa buru, eni ace anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa buru?

34. Ndipo anati, Ambuye amfuna iye.

35. Ndipo anadzanave kwa Yesu; ndipo anayalika zobvala zao pa mwana wa buruyo, nakwezapo Yesu.

36. Ndipo pakupita iye, anayala zobvala zao m'njira.

Werengani mutu wathunthu Luka 19