Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo anati kwa iwo akuimirirapo, Mcotsereni ndalamayo, nimuipatse kwa iye wakukhala nazo ndalama khumi.

25. Ndipo anati kwa iye, Mbuye, ali nazo ndalama khumi.

26. Ndinena ndi inu, kuti kwa yense wakukhala naco kudzapatsidwa; koma kwa iye amene alibe kanthu, cingakhale cimene ali naco cidzacotsedwa.

27. Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani cao kuno, nimuwaphe pamaso panga,

28. Ndipo m'mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

29. Ndipo kunali, m'mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri lochedwa la Azitona, anatuma awiri a ophunzira,

Werengani mutu wathunthu Luka 19