Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. ndipo Iye anali mkulu wa amisonkho, nali wacuma.

3. Ndipo anafuna kuona Yesu ndiye uti, ndipo sana the, cifukwa ca khamulo, pakuti anali wamfupi msinkhu.

4. Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona iye; pakuti anati apite njira yomweyi.

5. Ndipo m'mene anadza pamalopo Yesu anakweza maso nati kwa iye, Zakeyu, fulumira, nutsike; pakuti lero ndiyenera kukhala m'nyumba mwako.

6. Ndipo anafulumira, natsika, namlandira iye wokondwera.

7. Ndipo m'mene anaciona anadandaula onse, nanena, Analowa amcereze munthu ali wocimwa.

Werengani mutu wathunthu Luka 19