Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:17-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo anati kwa iye, Cabwino, kapolo wabwino iwe; popeza unakhala wokhulupirika m'cacing'onong'ono, khala nao ulamuliro pa midzi khumi.

18. Ndipo anadza waciwiri, nanena, Mbuye, ndalama yanu yapindula ndalama zisanu.

19. Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza midzi isanu.

20. Ndipo wina anadza, nanena, Mbuye, taonani, siyi ndalama yanu, ndaisunga m'kansaru;

21. pakuti ndinakuopani, popeza inu ndinu munthu wouma mtima: munyamula cimene simunaciika pansi, mututa cimene simunacifesa.

22. Ananena kwa iye, Pakamwa pako ndikuweruza, kapolo woipa iwe. Unadziwa kuti ine ndine munthu wouma mtima, wonyamula cimene sindinaciika, ndi wotuta cimene sindinacifesa;

23. ndipo sunapereka bwanji ndalama yanga pokongoletsa, ndipo ine pakudza ndikadaitenga ndi phindu lace?

24. Ndipo anati kwa iwo akuimirirapo, Mcotsereni ndalamayo, nimuipatse kwa iye wakukhala nazo ndalama khumi.

25. Ndipo anati kwa iye, Mbuye, ali nazo ndalama khumi.

26. Ndinena ndi inu, kuti kwa yense wakukhala naco kudzapatsidwa; koma kwa iye amene alibe kanthu, cingakhale cimene ali naco cidzacotsedwa.

27. Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani cao kuno, nimuwaphe pamaso panga,

28. Ndipo m'mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

29. Ndipo kunali, m'mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri lochedwa la Azitona, anatuma awiri a ophunzira,

30. nati, Mukani ku mudzi uli pandunji panu; m'menemo, polowa, mudzapeza mwana wa buru womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iri yonse; mummasule iye nimumtenge.

31. Ndipomunthuakati kwa inu, Mummasuliranji? mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32. Ndipo anacoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

Werengani mutu wathunthu Luka 19