Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 18:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo m'mudzimo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.

4. Ndipo sanafuna nthawi; koma bwino bwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;

5. koma cifukwa ca kundibvuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwace.

6. Ndipo Ambuye anati, Tamverani conena woweruza wosalungama.

Werengani mutu wathunthu Luka 18