Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 18:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo m'mudzimo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.

4. Ndipo sanafuna nthawi; koma bwino bwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;

5. koma cifukwa ca kundibvuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwace.

6. Ndipo Ambuye anati, Tamverani conena woweruza wosalungama.

7. Ndipo kodi Mulungu sadzacitira cilungamo osankhidwa ace akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?

8. Ndinena ndi inu, adzawacitira cilungamo posacedwa. Koma Mwana wa munthu pakudza Iye, vadzapeza cikhulupiriro pa dziko lapansi kodi?

9. Ndipo anatinso kwa ena amene anadzikhulupirira mwa iwo okha kuti ali olungama, napeputsa onse ena, fanizo ili,

10. Anthu awiri anakwera kunka kukacisi kukapemphera; winayo Mfarisi ndi mnzace wamsonkho.

11. Mfarisiyo anaimirira napemphera izi mwa yekha, Mulungu, ndikuyamikani kuti sindiri monga anthu onse ena, opambapamba, osalungama, acigololo, kapenanso monga wamsonkho uyu;

Werengani mutu wathunthu Luka 18