Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 18:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. ndisala cakudya kawiri sabata limodzi; ndipereka limodzi lamagawo khumi la zonse ndiri nazo.

13. Koma wamsonkhoyo alikuima patali sanafuna kungakhale kukweza maso kumwamba, komatu anadziguguda pacifuwa pace nanena, Mulungu, mundicitire cifundo, ine wocimwa.

14. Ndinena ndi inu, anatsikira kunyumba kwace woyesedwa wolungama uyutu, wosati uja ai; pakuti yense wakudzikuza yekha adzacepetsedwa; koma wodzicepetsa yekha adzakulitsidwa.

15. Ndipo anadzanao kwa iye ana amakanda kuti awakbudze; koma pamene ophunzira anaona, anawadzudzula.

16. Koma Yesu anawaitana, nanena, Lolani ana adze kwa Ine, ndipo musawaletse; pakuti Ufumu wa Mulungu uti wa otere.

17. Indetu ndinena kwa inu, Ali yense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati mwana, sadzalowamo ndithu.

18. Ndipo mkuru wina anamfunsa iye, nanena, Mphunzitsi wabwino, ndizicita ciani, kuti ndilowe moyo wosatha?

19. Koma Yesu anati kwa iye, Undicha Ine wabwino bwanji? palibe wabwino, koma mmodzi, ndiye Mulungu.

20. Udziwa malamulo. Usacite cigololo, Usaphe, Usabe, Usacite umboni wonama, Lemekeza atate wako ndi amako.

Werengani mutu wathunthu Luka 18