Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 17:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. wosanena naye makamaka, Undikonzere cakudya me, nudzimangire, nunditumikire kufikira ndadya ndi kumwa; ndipo nditatha ine udzadya nudzamwa iwe?

9. Kodi ayamika kapoloyocifukwa anacita zolamulidwa?

10. Cotero Inunso m'mene mutacita zonse anakulamulirani, Denani, Ife ndife akapolo opanda pace, tangocita zimene tayenera kuzicita.

11. Ndipo kunali, pakumuka ku Yerusalemu iye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.

12. Ndipo m'mene analowa iye m'mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;

13. ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, muticitire cifundo.

14. Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m'kumuka kwao, anakonzedwa.

15. Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anaciritsidwa, anabwerera m'mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau akuru;

16. ndipo anagwa nkhope yace pansi ku mapazi ace, namyamika iye; ndipo anali Msamariya ameneyo.

17. Ndipo Yesu anayankha nati, Kodi sanakonzedwa khumi? koma ali kuti asanu ndi anai aja?

18. Akubwera kulemekeza Mulungu sanapezeka mmodzi kodi, koma mlendo uyu?

19. Ndipo anati kwa iye, Nyamuka, nupite; cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe.

Werengani mutu wathunthu Luka 17