Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 17:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anati kwa ophunzira ace, Sikutheka kuti zolakwitsa zisadze; koma tsoka iye amene adza nazo.

2. Kukolowekedwa mwala wamphero m'khosi mwace ndi kuponyedwa Iye m'nyanja nkwapafupi, koma kulakwitsa mmodzi wa ang'ono awa nkwapatali.

3. Kadzicenjerani nokha; akacimwa mbale wako umdzudzule; akalapa, umkhululukire.

4. Ndipo akakucimwira kasanu ndi kawiri pa tsiku lace, nakakutembenukira kasanu ndi kawiri ndi kunena, Ndalapa ine; uzimkhululukira.

5. Ndipo atumwi anati kwa Ambuye, Mutionjezere cikhulupiriro.

6. Koma Ambuye anati, Mukakhala naco cikhulupiriro ngati kambeu kampiru, mukanena kwa mtengo uwu wamkuyu, Uzulidwe, nuokedwe m'nyanja; ndipo ukadamvera inu.

Werengani mutu wathunthu Luka 17