Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 16:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo Ine ndinena kwa inu, Mudziyesere nokha abwenzi ndi cuma cosalungama; kuti pamene cikakusowani, iwo akalandire inu m'mahema osatha.

10. Iye amene akhulupirika m'cacing'onong'ono alinso wokhulupirika m'cacikuru; ndipo iye amene ali wosalungama m'cacing'onong'ono alinso wosalungama m'cacikuru.

11. Cifukwa cace ngati simunakhala okhulupirika m'cuma ca cosalungama, adzakhulupirira inu ndani ndi cuma coona?

12. Ndipo ngati simunakhala okhulupirika ndi zace za wina, adzakupatsani inu ndani za inu eni?

Werengani mutu wathunthu Luka 16