Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

6. Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.

7. Ndipo iye ananena fanizo kwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,

Werengani mutu wathunthu Luka 14