Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:20-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo anati wina, Ine ndakwatira mkazi, ndipo cifukwa cace sindingathe kudza.

21. Ndipo kapoloyo pakubwera anauza mbuye wace zinthu izi. Pamenepo mwini nyumba anakwiya, nati kwa kapolo wace, Turuka msanga, pita kumakwalala ndi ku njira za mudzi, nubwere nao muno aumphawi ndi opunduka ndi akhungu ndi otsimphina.

22. Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, cimene munacilamulira cacitika, ndipo malo atsalapo.

23. Ndipo mbuye ananena kwa kapoloyo, Turuka, nupite kumiseu ndi njira za kuminda, nuwaumirize anthu alowe, kuti nyumba yanga idzale.

24. Pakuti ndinena kwa inu, kuti kulibe mmodzi wa amuna oitanidwa aja adzalawa phwando langa.

25. Ndipo mipingo yambiri ya anthu inamuka naye; ndipo iye anapotoloka, nati kwa iwo.

26. Munthu akadza kwa Ine, wosada atate wace ndi amace, ndi mkazi wace, ndi ana, ndi abale, ndi alongo ace, inde ndi moyo wace womwe wa iye mwini, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

27. Ndipo amene ali yense sasenza mtanda wace wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sakhoza kukhala wophunzira wanga,

28. Pakuti ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja yaitali, sathanga wakhala pansi, nawerengera mtengo wace, aone ngati ali nazo zakuimariza?

29. Kuti kungacitike, pamene atakhazika pansi miyala ya ku maziko ace, osakhoza kuimariza, anthu onse akuyang'ana adzayamba kumseka iye,

30. ndi kunena kuti, Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumariza.

Werengani mutu wathunthu Luka 14