Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali pamene iye analowa m'nyumba ya mmodzi wa akuru a Afarisi tsiku la Sabat a, kukadya, iwo analikumzonda iye.

2. Ndipo onani, panali pamaso pace munthu wambulu.

3. Ndipo Yesu anayankha nati kwa acilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuciritsa, kapena iai?

4. Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

6. Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.

7. Ndipo iye ananena fanizo kwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,

8. Pamene pali ponse waitanidwa iwe ndi munthu ku cakudya ca ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,

Werengani mutu wathunthu Luka 14