Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 14:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali pamene iye analowa m'nyumba ya mmodzi wa akuru a Afarisi tsiku la Sabat a, kukadya, iwo analikumzonda iye.

2. Ndipo onani, panali pamaso pace munthu wambulu.

3. Ndipo Yesu anayankha nati kwa acilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuciritsa, kapena iai?

4. Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

Werengani mutu wathunthu Luka 14