Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 12:22-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo Iyeanati kwa ophunzira ace, Cifukwa cace ndinena ndinu, Musade nkhawa ndi moyo wanu, cimene mudzadya; kapena ndi thupi lanu, cimene mudzabvala.

23. Pakuti moyo uli woposa cakudya, ndi thupi liposa cobvala.

24. Lingirirani makungubwi, kuti samafesai, kapena kutemai; alibe nyumba yosungiramo, kapena nkhokwe; ndipo Mulungu awadyetsa: nanga inu simuziposa mbalame kwambiri!

25. Ndipo ndani wa inu, ndi kuda nkhawa angathe kuonjeza mkono pa msinkhu wace?

26. Kotero ngati simungathe ngakhale cacing'onong'ono, muderanji nkhawa cifukwa ca zina zija?

27. Lingalirani maluwa, makulidwe ao; sagwiritsa nchito ndi kusapota; koma ndinena kwa inu, Ngakhale Solomo, mu ulemerero wace wonse, sanabvala ngati limodzi la awa.

28. Koma ngati Mulungu abveka kotere maudzu a kuthengo akukhala lero, ndipo mawa aponyedwa pamoto; nanga inu sadzakuninkhani koposa, inu okhulupirira pang'ono?

29. Ndipo inu musafunefune cimene mudzadya, ndi cimene mudzamwa; ndipo musakayike mtima.

Werengani mutu wathunthu Luka 12