Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 12:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Koma kulibe kanthu kobvundikiridwa kamene sikadzaululidwa; ndi kobisika kamene sikadzadziwika.

3. Cifukwa cace zonse zimene mwazinena mumdima zidzamveka poyera; ndipo cimene mwalankhula m'khutu, m'zipinda za m'kati cidzalalikidwa pa macindwi a nyumba.

4. Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ici alibe kanthu kena angathe kucita.

5. Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya kugehena, inde, ndinena ndinu opani ameneyo.

6. Kodi mpheta zisanu sizigulidwa timakobiri tiwiri? ndipo palibe imodzi ya izo iiwalika pamaso pa Mulungu;

7. komatu ngakhale matsitsi onse a pamutu panu awerengedwa. Musaopa, muposa mtengo wace wa mpheta zambiri.

8. Ndipo ndinena kwa inu, Amene ali yense akabvomereza Ine pamaso pa anthu, inde, Mwana wa munthu adzambvomereza iye pamaso pa angelo a Mulungu;

9. koma iye wondikana Ine pamaso pa anthu, iye adzakanidwa pamaso pa angelo a Mulungu.

10. Ndipo amene ali yense adzanenera Mwana wa munthu zoipa adzakhululukidwa; koma amene anenera Mzimu Woyera zamwano sadzakhululukidwa.

11. Ndipo pamene pali ponse adzamuka nanu ku mlandu wa m'sunagoge ndi kwa akulu, ndi aulamuliro, musade nkhawa ndi kuti mukadzikanira bwanji, ndipo ndi mau otani, kapena mukanena ciani;

12. pakuti Mzimu Woyera adzaphunzitsa inu nthawi yomweyo zimene muyenera kuzinena.

Werengani mutu wathunthu Luka 12