11. Ndipo pamene pali ponse adzamuka nanu ku mlandu wa m'sunagoge ndi kwa akulu, ndi aulamuliro, musade nkhawa ndi kuti mukadzikanira bwanji, ndipo ndi mau otani, kapena mukanena ciani;
12. pakuti Mzimu Woyera adzaphunzitsa inu nthawi yomweyo zimene muyenera kuzinena.
13. Ndipo munthu wa m'khamulo anati kwa iye, Mphunzitsi, uzani mbale wanga agawane ndi ine cuma camasiye.