Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 12:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pomwepo pamene anthu a zikwi zikwi a khamu anasonkhana pamodzi, kotero kuti anapondana, iye anayamba kunena kwa ophunzira ace poyamba, Tacenierani nokha ndi cotupitsa mikate ca Afarisi, cimeneciri cinyengo.

2. Koma kulibe kanthu kobvundikiridwa kamene sikadzaululidwa; ndi kobisika kamene sikadzadziwika.

3. Cifukwa cace zonse zimene mwazinena mumdima zidzamveka poyera; ndipo cimene mwalankhula m'khutu, m'zipinda za m'kati cidzalalikidwa pa macindwi a nyumba.

4. Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ici alibe kanthu kena angathe kucita.

5. Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya kugehena, inde, ndinena ndinu opani ameneyo.

Werengani mutu wathunthu Luka 12