Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu adzakhala ndi bwenzi lace, nadzapita kwa iye pakati pa usiku, nadzati kwa iye, Bwenzi, ndibwereke mikate itatu;

6. popeza wandidzera bwenzi langa locokera paulendo, ndipo ndiribe compatsa;

7. ndipo iyeyu wa m'katimo poyankha akati, Usandibvuta; pakhomo mpotseka tsopano, ndipo ana anga ali nane pamodzi pogona; sindikhoza kuuka ndi kukupatsa?

8. Ndinena ndi inu, ngakhale sadzauka ndi kumpatsa, cifukwa ali bwenzi lacevkoma cifukwa ca liuma lace adzauka nadzampatsa iye ziri zonse azisowa.

9. Ndipo Ine ndinena ndi inu, Pemphani, ndipo adzakupatsani; funani, ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsegulirani.

10. Pakuti yense wakupempha alandira; ndi wofunayo apeza; ndi iye amene agogoda adzamtsegulira.

Werengani mutu wathunthu Luka 11