Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:32-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Momwemonso Mlevi, pofika pamenepo, ndi kumuona, anapita mbali yina.

33. Koma Msamariya wina ali pa ulendo wace anadzapali iye; ndipo pakumuona, anagwidwa cifundo,

34. nadza kwa iye, namanga mabala ace, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yace ya iye yekha, nadza naye ku nyumba ya alendo, namsungira.

35. Ndipo m'mawa mwace anaturutsa marupiya atheka awiri napatsa mwini nyumba ya alendo, nati, Msungire iye, ndipo ciri conse umpatsa koposa, ine, pobwera, ndidzakubwezera iwe.

36. Uti wa awa atatu, uyesa iwe, anakhala mnansi wa iye uja adagwa m'manja a acifwamba?

37. Ndipo anati, iye wakumcitira cifundo. Ndipo Yesu anati kwa iye, Pita, nucite iwe momwemo.

38. Ndipo pakupita paulendo pao iye analowa m'mudzi wina; ndipo mkazi wina dzina lace 4 Marita anamlandira iye kunyumba kwace.

39. Ndipo anali ndi mbale wace wochedwa Mariya, ndiye wakukhala pa mapazi a Ambuye, namva mau ace.

40. Koma Marita anatekeseka ndi kutumikira kwambiri; ndipo anadzako nati, Ambuye, kodi simusamala kuti mbale wanga anandisiya nditumikire ndekha? Mumuuze tsono kuti andithandize.

41. Koma Ambuye anayankha nati kwa iye, Marita, Marita, uda nkhawa nubvutika ndi zinthu zambiri;

42. koma cisoweka cinthu cimodzi, pakuti Mariya anasankha dera lokoma limene lsilidzacotsedwa kwa iye.

Werengani mutu wathunthu Luka 10